5. Ndipo Mulungu wanga anaika m'mtima mwanga kuti ndiwasonkhanitse aufuru, ndi olamulira, ndi anthu, kuti awerengedwe mwa cibadwidwe cao. Ndipo ndinapeza buku la cibadwidwe la iwo adakwerako poyamba paja; ndinapeza mudalembedwa m'mwemo.
6. Ana a dziko amene anakwera kucokera kundende a iwo adatengedwa ndende, amene Nebukadinezara mfumu ya Babulo adawatenga, anabwera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, yense ku mudzi wace, ndi awa:
7. ndiwo amene anadza ndi Zerubabele: Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Moredekai, Bilisani, Misiperete, Bigivai, Nehumu, Baana. Mawerengedwe a amuna a anthu Aisrayeli ndiwo:
8. ana a Parosi zikwi ziwiri mphambu zana limodzi kudza makumi asanu ndi awiri.
9. Ana a Sefatiya, mazana atatu mphambu makumi asanu ndi awiri kudza awiri.
10. Ana a Ara, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu kudza awiri.
11. Ana a Pakati Moabu, a ana a Yesuwa ndi Yoabu, zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi atatu kudza khumi limodzi ndi asanu ndi atatu.
12. Ana a Elamu, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri ndi makumi asanu kudza anai.