15. Ndipo anampeza munthu, taonani, analinkusokera m'thengo; munthuyo ndipo anamfunsa, nati, Kodi ufuna ciani?
16. Ndipo iye anati, Ndifuna abale anga. Undiuzetu kumene adyetsa zoweta.
17. Munthuyo ndipo anati, Anacoka pano; pakuti ndinamva alinkuti, Timuke ku Dotana. Yosefe ndipo anatsata abale ace, nawapeza ali ku Dotana.
18. Ndipo iwo anamuona iye ali patari, ndipo asanayandikire pafupi ndi iwo, anampangira iye ciwembu kuti amuphe.
19. Ndipo anati wina ndi mnzace, Taonani, alinkudza mwini maloto uja.