Caka caciwiri tsono cakufika iwo ku nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu, mwezi waciwiri, Zerubabele mwana wa Sealitiyeli, ndi Yesuwa mwana wa Yozadaki, ndi abale ao otsala, ansembe ndi Alevi ndi onse ocokera kundende kudza ku Yerusalemu, anayamba, naika Alevi a zaka makumi awiri ndi mphambu, ayang'anire nchito ya nyumba ya Yehova.