5. Pomwepo Abisalomu anati, Kaitane tsopano Husai M-ariki yemwe, timvenso cimene anene iye.
6. Ndipo pakufika Husai kwa Abisalomu, Abisalomuyo ananena naye, Ahitofeli analankhula mau akuti; ticite kodi monga mwa kunena kwace? ngati iai, unene ndiwe.
7. Ndipo Husai ananena ndi Abisalomu, Uphungu anaupangira lero Ahitofeli suli wabwino.