11. Pomwepo Davide anagwira zobvala zace nazing'amba; nateronso anthu onse okhala naye.
12. Nabuma, nalira misozi, nasala kudya kufikira madzulo, cifukwa ca Sauli ndi mwana wace Jonatani, ndi anthu a Yehova, ndi banja la Israyeli, cifukwa adagwa ndi lupanga.
13. Ndipo Davide ananena ndi mnyamata wakumuuzayo, Kwanu nkuti? Nayankha, Ine ndine mwana wa mlendo, M-amaleki.
14. Ndipo Davide ananena naye, Bwanji sunaopa kusamula dzanja lako kuononga wodzozedwa wa Yehova?
15. Davide naitana wina wa anyamatawo, nati, Sendera numkanthe, Ndipo anamkantha, nafa iye.