29. Itero mfumu, Asakunyengeni Hezekiya; pakuti sadzakhoza kukulanditsani m'dzanja lace;
30. kapena Hezekiya asakukhulupiritseni pa Yehova, ndi kuti, Yehova adzatilanditsa ndithu, ndi mudzi uwu sudzaperekedwa m'dzanja la mfumu ya Asuri.
31. Musamvere Hezekiya; pakuti Itero mfumu ya Asuri, Mupangane nane zamtendere, nimuturukire kwa ine, ndi kumadya yense ku mpesa wace, ndi yense ku mkuyu wace, ndi kumwa yense madzi a m'citsime cace;