28. Ndipo Sauli anaona, nadziwa kuti Yehova ali ndi Davide; ndi kuti Mikala mwana wa Sauli anamkonda Davide.
29. Sauli nayamba kumuopa Davide kopambana; ndi Sauli anali mdani wa Davide masiku onse.
30. Pomwepo mafumu a Afilisti anaturuka; ndipo nthawi zonse anaturuka iwo, Davide anali wocenjera koposa anyamata onse a Sauli, comweco dzina lace linatamidwa kwambiri.