Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 8:13-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Cifukwa cace Afarisi anati kwa iye, Mucita umboni wa Inu nokha; umboni wanu suli woona.

14. Anayankha Yesu nati kwa iwo, Ndingakhale ndicita umboni wa Ine ndekha umboni wanga uli woona; cifukwa ndidziwa kumene ndinacokera ndi kumene ndimukako; koma e inu, simudziwa kumene ndicokera, ndi kumene ndimukako.

15. Inu muweruza monga mwa thupi; Ine sindiweruza munthu.

16. Ndipo ngati ndiweruza Ine, ciweruziro canga ciri coona; pakuti sindiri pa ndekha, koma ine ndi Atate amene anandituma Ine.

17. Inde kudalembedwa m'cilamulo canu kuti umboni wa anthu awiri uli woona.

18. Ine ndine wakucita umboni wa Ine ndekha, ndipo Atate amene anandituma Ine, acita umboni wa Ine.

19. Cifukwa cace ananena ndi iye, Ali kuti Atate, wanu? Yesu anayankha, Simudziwa kapena Ine, kapena Atate wanga; mukadadziwa Ine, mukada-dziwanso Atate wanga.

20. Mau awa analankhula m'nyumba ya cuma ca Mulungu pophunzitsa m'Kacisi; ndipo palibe munthu anamgwira iye, pakuti nthawi yace siinafike.

21. Pamenepo anatinso kwa iwo; Ndimuka Ine, ndipo mudzandifuna, ndipo m'cimo lanu mudzafa: kumene ndimukako Ine, simudziwa kudza inu.

Werengani mutu wathunthu Yohane 8