Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 7:8-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. K werani inu kunka kuphwando; sindikwera Ineku phwando ili tsopano apa; pakuti nthawi yanga siinakwanire.

9. Ndipo m'mene adanena nao zimenezi anakhalabe m'Galileya,

10. Koma pamene abale ace adakwera kunka kuphwando, pomwepo Iyenso anakwera, si poonekera, koma monga mobisalika.

11. Pomwepo Ayuda analikumfuna iye paphwando, nanena, Ali kuti uja?

12. Ndipo kunali kung'ung'udza kwambiri za iye m'makamu a anthu; ena ananena, kuti, Ali wabwino; koma ena ananena, lai, koma asoceretsa khamu la anthuwo.

13. Cinkana anatero panalibe munthu analankhula za iye poyera, cifukwa ca kuopa Ayuda.

Werengani mutu wathunthu Yohane 7