21. Yesu anayankha nati kwa iwo, Ndinacita nchito imodzi, ndipo muzizwa monse,
22. Cifukwa ca ici Mose, anakupatsani inu mdulidwe (si kuti ucokera kwa Mose, koma kwa, makolo); ndipo mudula munthu tsiku la Sabata.
23. Ngati munthu alandira mdulidwe tsiku la Sabata, kuti cilamulo ca Mose cingapasulidwe; kodi mundikwiyira Ine, cifukwa ndamciritsadi munthu tsiku la Sabata?
24. Musaweruze monga maonekedwe, koma weruzani ciweruziro colungama.