Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 7:20-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Khamu la anthu linayankha, Muli ndi ciwanda: afuna ndani kukuphani lou?

21. Yesu anayankha nati kwa iwo, Ndinacita nchito imodzi, ndipo muzizwa monse,

22. Cifukwa ca ici Mose, anakupatsani inu mdulidwe (si kuti ucokera kwa Mose, koma kwa, makolo); ndipo mudula munthu tsiku la Sabata.

23. Ngati munthu alandira mdulidwe tsiku la Sabata, kuti cilamulo ca Mose cingapasulidwe; kodi mundikwiyira Ine, cifukwa ndamciritsadi munthu tsiku la Sabata?

24. Musaweruze monga maonekedwe, koma weruzani ciweruziro colungama.

Werengani mutu wathunthu Yohane 7