Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 7:15-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Cifukwa cace Ayuda anazizwa, nanena, Ameneyu adziwa bwanji zolemba, wosaphunzira?

16. Pamenepo Yesu anayankha iwo, nati, Ciphunzitso canga siciri canga, koma ca iye amene anandituma Ine.

17. Ngati munthu ali yense afuna kucita cifuniro cace, adzazindikira za ciphunzitsoco, ngati cicokera kwa Mulungu, kapena ndilankhula zocokera kwa Ine ndekha.

18. Iye wolankhula zocokera kwa iye yekha afuna ulemu wa mwini yekha, iye wakufuna ulemu wa iye amene anamtuma, yemweyu ali woona, ndipo mwa iye mulibecosalungama.

19. Si Mose kodi anakupatsani inu cilamulo, ndipo kulibe mmodzi mwa inu acita cilamulo? Mufuna kundipha cifukwa ninji?

20. Khamu la anthu linayankha, Muli ndi ciwanda: afuna ndani kukuphani lou?

21. Yesu anayankha nati kwa iwo, Ndinacita nchito imodzi, ndipo muzizwa monse,

22. Cifukwa ca ici Mose, anakupatsani inu mdulidwe (si kuti ucokera kwa Mose, koma kwa, makolo); ndipo mudula munthu tsiku la Sabata.

23. Ngati munthu alandira mdulidwe tsiku la Sabata, kuti cilamulo ca Mose cingapasulidwe; kodi mundikwiyira Ine, cifukwa ndamciritsadi munthu tsiku la Sabata?

Werengani mutu wathunthu Yohane 7