43. Yesu anayankha nati kwa iwo, Musang'ung'udze winandi mnzace.
44. Kulibe mmodzi akhoza kudza kwa Ine koma ngati Atate wondituma Ine amkoka iye; ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomariza.
45. Calembedwa mwa aneneri, Ndipo adzakhala onse ophunzitsidwa ndi Mulungu. 1 Yense amene adamva kwa Atate, naphunzira, adza kwa Ine.
46. 2 Sikuti munthu wina waona Atate, koma 3 iye amene ali wocokera kwa Mulungu, ameneyo waona Atate.
47. Indetu, indetu, ndinena ndi inu, 4 iye wokhuluplra ali nao moyo wosatha.
48. 5 Ine ndine mkate wamoyo,
49. 6 Makolo anu adadya m'cipululu, ndipo adamwalira.
50. 7 Mkate wotsika Kumwamba ndi uwu, kuti munthu akadyeko ndi kusamwalira.
51. 8 Mkate wamoyo wotsika Kumwamba Ndine amene. Ngati munthu wina akadyako mkate umene, adzakhala ndi moyo kosatha. Inde, ndipo 9 mkate umene ndidzapatsa Ine, ndiwo thupi langa, ukhale moyo wa dziko lapansi.
52. Pamenepo Ayuda anatetana wina ndi mnzace ndi kunena, Akhoza bwanji ameneyu kutipatsa ife kudya thupi lace?