31. Ngati ndicita umboni wa Ine ndekha, umboni wanga suli woona.
32. Wocita umboni wa Ine ndi wina; ndipo ndidziwa kuti umboni umene iye andicitira Ine uli woona.
33. Inu munatuma kwa Yohane, ndipo iye anacitira umboni coonadi.
34. Ndipo Ine sindilandira umboni kwa munthu: koma ndinena izi, kuti inu mukapulumutsidwe.
35. Iyeyo anali nyali yoyaka ndi yowala; ndipo inu munafuna kukondwera m'kuunika kwace kanthawi.