Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 5:27-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. ndipo anampatsa iye mphamvu ya kucita mlandu, pakuti ali Mwana wa munthu.

28. Musazizwe ndi ici, kuti ikudza nthawi, imene onse ali m'manda adzamva mau ace,

29. nadzaturukira, amene adacita zabwino, kukuuka kwa moyo; koma amene adacita zoipa kukuuka kwa kuweruza.

30. Sindikhoza kucita kanthu kwa Ine ndekha; monga momwe ndimva ndiweruza; ndipo maweruzidwe anga ali olungama; cifukwa kuti sinditsata cifuniro canga, koma cifuniro ca Iye ondituma Ine.

31. Ngati ndicita umboni wa Ine ndekha, umboni wanga suli woona.

32. Wocita umboni wa Ine ndi wina; ndipo ndidziwa kuti umboni umene iye andicitira Ine uli woona.

33. Inu munatuma kwa Yohane, ndipo iye anacitira umboni coonadi.

34. Ndipo Ine sindilandira umboni kwa munthu: koma ndinena izi, kuti inu mukapulumutsidwe.

35. Iyeyo anali nyali yoyaka ndi yowala; ndipo inu munafuna kukondwera m'kuunika kwace kanthawi.

36. Koma Ine ndiri nao umboni woposa wa Yohane; pakuti nchito zimene Atateanandipatsa ndizitsirize, nchito zomwezo ndizicita zindicitira umboni, kuti Atate anandituma Ine.

37. Ndipo Atate wonditumayo, 1 Iyeyu wandicitira Ine umboni. Simunamva mau ace konse, kapena maonekedwe ace simunaona.

38. Ndipo mulibe mau ace okhala mwa inu; cifukwa kuti amene Iyeyu anatuma, inu simumkhulupirira ameneyo.

39. 2 Musanthula m'malembo, popeza muyesa kuti momwemo muli nao moyo wosatha; ndipo akundicitira Ine umboni ndi iwo omwewo;

40. ndipo 3 simufuna kudza kwa Ine, kuti mukhale nao moyo.

41. 4 Ulemu sindiulandira kwa anthu.

42. Koma ndikudziwani inu, kuti mulibe cikondiea Mulungu mwa inu nokha.

Werengani mutu wathunthu Yohane 5