Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 5:14-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Zitapita izi Yesu anampeza m'Kacisi, nati kwa iye, Taona, waeiritsidwa; usacimwenso, kuti cingakugwere ecipa coposa.

15. Munthuyo anacoka, nauza Ayuda, kuti ndiye Yesu amene adameiritsa.

16. Ndipo cifukwa ca ici Ayuda analondalonda Yesu, popeza anacita izo dzuwa la Sabata.

17. Koma Yesu anayankha iwo, Atate wanga amagwira nchito kufikira tsopano, lnenso ndigwira nchito.

18. Cifukwa ca ici Ayuda anaonjeza kufuna kumupha, si cifukwa ca kuswa dzuwa la Sabata kokha, komatu amaehanso Mulungu Atate wace wa iye yekha; nadziyesera wolingana ndi Mulungu.

19. Pamenepo Yesu anayankha nati kwa iwo, Indetu, indetu, ndinena kwa inu, sakhoza Mwana kucita kanthu pa yekha, koma cimene aona Atate acicita, ndico. Pakuti zimene iye azicita, zomwezo Mwananso azicita momwemo.

20. Pakuti Atate akonda Mwana, namuonetsa zonse azicita yekha: ndipo adzamuonetsa nchito zoposa izi, kuti mukazizwe,

21. Pakuti monga Atate aukitsa akufa, nawapatsa moyo, momwemonso Mwanaapatsa moyo iwo amene iye afuna.

22. Pakuti Atate saweruza munthu ali yense, koma anapereka kuweruza konse kwa Mwana;

23. kuti onse akalemekeze Mwana, monga alemekeza Atate. Wosalemekeza Mwana salemekeza Atate amene anamtuma iye.

24. Indetu, indetu, ndinena kwa inu, kuti iye wakumva mau anga, ndi kukhulupirira iye amene anandituma Ine, ali nao moyo wosatha, ndipo salowa m'kuweruza, koma wacokera kuimfa, nalowa m'moyo.

25. Indetu, indetu, ndinena kwa inu, kuti ikudza nthawi, ndipo Iripo tsopano, imene akufa adzamva mau a Mulungu; ndipo iwo akumva adzakhala ndi moyo.

26. Pakuti monga Atate ali ndi moyo mwa iye yekha, momwemonso anapatsa kwa Mwana kukhala ndi moyo mwa iye yekha;

Werengani mutu wathunthu Yohane 5