Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 3:20-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Pakuti yense wakucita zoipa adana nako kuunika, ndipo sakudza kwa kuunika, kuti zingatsutsidwe nchito zace.

21. Koma wocita coonadi adza kukuunika, kuti nchito zace zionekere kuti zinacitidwa mwa Mulungu.

22. Zitapita in anadza Yesu ndi akuphunzira ace ku dziko la Yudeya; ndipo pamenepo anatsotsa nao pamodzi, nabatiza.

23. Ndipo Yohane analinkubatiza m'Ainoni pafupi pa Salemu, cifukwa panali madzi ambiri pamenepo; ndipo analinkufikako anthu, nalinkubatizidwa.

24. Pakuti Yohane sanaikidwe m'ndende.

25. Pamenepo padauka kufunsana mwa ophunzira ace a Yohane ndi Myuda za mayeretsedwe.

26. Ndipo anadza kwa Yohane, nati kwa iye, Rabi, Iye amene anali ndi inu tsidya lija la Y ordano, amene munamcitira umboni, taonani yemweyu abatiza, ndipo anthu onse alinkudza kwa iye.

27. Yohane anayankha nati, Munthu sakhoza kulandira kanthu, ngati sikapatsidwa kwa iye kocokera Kumwamba.

28. Inu nokha mundicitira umboni, kuti ndinati, Sindine Kristu, koma kuti ndiri wotumidwa m'tsogolo mwace mwa iye.

29. Iye amene ali naye mkwatibwi ali mkwati, koma mnzace wa mkwatiyo, wakuimirira ndi kumvera iye, akondwera kwakukuru cifukwa ca mau a mkwatiyo; cifukwa cace cimwemwe canga cimene cakwanira.

30. Iyeyo ayenera kukula koma ine ndicepe.

31. Iye wocokera Kumwamba ali woposa onse; iye amene ali wa dziko lapansi ali wa dziko lapansi, nalankhula za dziko lapansi: Iye wocokera Kumwamba ali woposa onse.

32. Cimene anaciona nacimva, acita umboni wa ici comwe; ndipo kulibe munthu alandira umboni wace.

33. 1 Iye amene analandira umboni wace anaikapo cizindikilo cace kuti Mulungu ali woona.

34. Pakuti 2 Iye amene Mulungu anamtuma alankhula mau a Mulungu; pakuti 3 sapatsa Mzimu ndi muyeso.

35. 4 Atate akonda Mwana, nampatsa zinthu zonse m'dzanja lace.

Werengani mutu wathunthu Yohane 3