Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 21:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Zitapita izi Yesu anadzionetseranso kwa akuphunzira ace ku nyanja ya Tiberiya. Koma anadzionetsera cotere.

2. Anali pamodzi Simoni Petro, ndi Tomasi, wochedwa Didimo, ndi Natanayeli wa ku Kana wa ku Galileya, ndi ana a Zebedayo, ndi awiri ena a akuphunzira ace.

3. Simoni Petro ananena nao, ndinka kukasodza. Ananena naye, Ifenso tipita nawe. Anaturuka, nalowa m'ngalawa; ndipo m'usiku muja sanagwira kanthu.

4. Koma pakuyamba kuca, Yesu anaimirira pam bali pa nyanja, komatu akuphunzirawo sanadziwa kuti ndiye Yesu.

5. Yesu ananena nao, Ananu, muli nako kanthu kakudya kodi? Anamyankha iye, lai.

Werengani mutu wathunthu Yohane 21