Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 20:20-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo pamene adanena ici, anaonetsa iwo manja ace ndi nthiti zace. Pamenepo akuphunzira anakondwera pakuona Ambuye.

21. Cifukwa cace Yesu anatinso kwa iwo, Mtendere ukhale ndi inu; monga Atate wandituma Ine, Inenso ndituma inu.

22. Ndipo pamene anati ici anawapumira, nanena nao, Landirani Mzimu Woyera.

23. Zocimwa za anthu ali onse muwakhululukira, zikhululukidwa kwa iwo; za iwo amene muzigwiritsa, zagwiritsidwa.

24. Koma Tomasi, mmodzi wa khumi ndi awiriwo, wochedwa Didimo, sanakhala nao pamodzi, pamene Yesu anadza.

25. Cifukwa cace akuphunzira ena ananena naye, Tamuona Ambuye. Koma iye anati kwa iwo, Ndikapanda kuona m'manja ace cizindikilo ca misomaliyo, ndi kuika cala canga m'cizindikilo ca misomaliyo, ndi kuika dzanja langa ku nthiti yace; sindidzakhulupira.

Werengani mutu wathunthu Yohane 20