Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 19:22-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Pilato anayankha, Cimene ndalemba, ndalemba.

23. Pamenepo asilikari, m'mene adapacika Yesu, anatenga zobvala zace, nadula panai, natenga wina cina, wina cina, ndiponso maraya; koma maraya anaombedwa monsemo kuyambira pamwamba pace, analibe msoko.

24. Cifukwa cace anati wina kwa mnzace, Tisang'ambe awa, koma ticite maere, awa akhale a yani; kuti lembo likwaniridwe limene linena, Anagawana zobvala zanga mwa iwo okha, ndi pa maraya anga anacitira maere. Ndipo asilikari anacita izi.

25. Koma pamtanda wa Yesu anaimirira amace, ndi mbale wa amace, Mariya, mkazi wa Kleopa, ndi Mariya wa Magadala.

26. Pamenepo Yesu pakuona amace, ndi wophunzira amene anamkonda, alikuimirirako, ananena kwa amace, Mkazi, taonani, mwana wanu!

27. Pamene ananena kwa wophunzirayo, Taona, amai wako. Ndipo kuyambira ora lomweli wophunzirayo ananka naye kwao.

28. Citapita ici Yesu, podziwa kuti zonse zidatha pomwepokuti lembo likwaniridwe, ananena, Ndimva ludzu.

29. Kunaikidwako cotengera codzala ndi vinyo wosasa; cifukwa cace anazenenga cinkhupule codzaza ndi vinyo wosasayo pa phesi lahisope, nacifikitsa kukamwa kwace.

30. Pamene Yesu tsono adalandira vinyo wosasayo anati, Kwatha; ndipo anawerama mutu, napereka mzimu.

31. Pomwepo Ayuda, popeza panali tsiku lokonzera, kuti 1 mitembo ingatsale pamtanda tsiku la Sabata, pakuti tsiku lomwelo la Sabata linali lalikuru, anapempha Pilato kuti miyendo yao ityoledwe, ndipo acotsedwe.

32. Cifukwa cace anadza asilikari natyola miyendo ya woyambayo, ndi ya winayo wopacikidwa pamodzi ndi iye;

33. koma pofika kwa Yesu, m'mene anamuona iye, kuti wafa kale, sanatyola miyendo yace;

34. koma mmodzi wa asilikari anamgwaza ndi nthungo m'nthiti yace, ndipo 2 panaturuka pomwepo mwazi ndi madzi.

35. Ndipo 3 iye amene anaona, wacita umboni, ndi umboni wace uti woona; ndipo iyeyu adziwa kuti anena zoona, kuti inunso mukakhulupire.

36. Pakuti izi zinacitika, kuti lembo likwaniridwe, 4 Pfupa la iye silidzatyoledwa.

37. Ndipo linenanso lembo lina, 5 Adzayang'ana pa iye amene anampyoza.

38. 6 Citatha ici. Y osefe wa ku Arimateya, ndiye wophunzira wa Yesu, koma mobisika, cifukwa ca kuopa Ayuda, anapempha Pilato kuti akacotse mtembo wa Yesu. Ndipo Pilato analola. Cifukwa cace anadza, nacotsa mtembo wace.

Werengani mutu wathunthu Yohane 19