Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 19:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo tsono Pilato anatenga Yesu, namkwapula.

2. Ndipo asilikari, m'mene analuka korona waminga anambveka pamutu pace, nampfunda iye maraya acibakuwa;

3. nadza kwa iye, nanena, Tikuoneni, Mfumu ya Ayuda! nampanda khofu.

4. Ndipo Pilato anaturukanso kunja, nanena nao, Taonani, ndidza naye kwa inu kunja kuti mudziwe kuti sindipeza mwa iye cifukwa ciri conse.

5. Pamenepo Yesu anaturuka kunja, atabvala korona waminga; ndi maraya acibakuwa, Ndipo ananena nao, Taonani munthuyu!

6. Ndipo pamene ansembe akulu ndi anyamata anamuona iye, anapfuula nanena, Mpacikeni, mpacikeni, Pilato ananena nao, Mtengeni iye inu nimumpaeike; pakuti ine sindipeza cifukwa mwa: iye.

Werengani mutu wathunthu Yohane 19