Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 18:20-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Yesu anayankha iye, Ine ndalankhula zomveka kwa dziko lapansi; ndinaphunzitsa Ine nthawi zonse m'sunagoge ndi m'Kacisi, kumene amasonkhana Ayuda onse; ndipo mobisika sindinalankhula kanthu.

21. Undifunsiranji Ine? funsa iwo amene adamva cimene ndinalankhula nao; taona, amenewo adziwa cimene ndinanena Ine.

22. Koma m'mene iye adanena izi, mmodzi wa anyamata akuimirirako anapanda Yesu khofu, ndi kuti, Kodi uyankha mkulu wa ansembe comweco?

23. Yesu anayankha iye, Ngati ndalankhula coipa, cita umboni wa coipaco, koma ngati bwino, undipandiranji?

24. Koma Anasi adamtumiza iye womangidwa kwa Kayafa mkulu wa ansembe.

25. Koma Simoni Petro analikuimirira ndi kuotha moto. Pomwepo anati kwa iye, Suli iwenso wa akuphunzira ace kodi? Iyeyu anakana, nati, Sindine.

Werengani mutu wathunthu Yohane 18