Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 12:45-49 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

45. Ndipo 9 wondiona Ine aona amene anandituma Ine

46. 10 Ndadza Ine kuunika ku dziko lapansi, kuti yense wokhulupirira Ine asakhale mumdima.

47. Ndipo ngati wina akumva mau anga, ndi kusawasunga, Ine sindimweruza; pakuti 11 sindinadza kudzaweruza dziko lapansi, koma kuti ndipulumutse dziko lapansi.

48. 12 iye amene akaniza Ine, ndi kusalandira mau anga, ali naye womweruza iye; 13 mau amene ndalankhula, iwowa adzamweruza tsiku lomariza.

49. 14 Pakuti sindinalankhula mwa Ine ndekha; koma Atate wondituma Ine, yemweyu anandipatsa Ine lamulo, limene ndikanene, ndi limene ndikalankhule.

Werengani mutu wathunthu Yohane 12