Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 12:39-50 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Cifukwa ca ici sanathe kukhulupira, pakuti Yesaya anatinso,

40. 4 Wadetsa maso ao, naumitsa mtima wao;Kuti angaone ndi maso, angazindikire ndi mtima,Nangatembenuke,Ndipo ndingawaciritse.

41. 5 Izi anati Yesaya, cifukwa anaona ulemerero wace; nalankhula za iye.

42. Kungakhale kotero, ambiri a mwa akuru anakhulupirira iye; koma 6 cifukwa ca Afarisi sanabvomereza, kuti angaletsedwe m'sunagoge,

43. 7 pakuti anakonda ulemerero wa anthu koposa ulemerero wa Mulungu.

44. Koma Yesu anapfuula nati, 8 iye wokhulupirira ine, sakhulupirira Ine, koma iye wondituma Ine.

45. Ndipo 9 wondiona Ine aona amene anandituma Ine

46. 10 Ndadza Ine kuunika ku dziko lapansi, kuti yense wokhulupirira Ine asakhale mumdima.

47. Ndipo ngati wina akumva mau anga, ndi kusawasunga, Ine sindimweruza; pakuti 11 sindinadza kudzaweruza dziko lapansi, koma kuti ndipulumutse dziko lapansi.

48. 12 iye amene akaniza Ine, ndi kusalandira mau anga, ali naye womweruza iye; 13 mau amene ndalankhula, iwowa adzamweruza tsiku lomariza.

49. 14 Pakuti sindinalankhula mwa Ine ndekha; koma Atate wondituma Ine, yemweyu anandipatsa Ine lamulo, limene ndikanene, ndi limene ndikalankhule.

50. Ndipo ndidziwa kuti lamulo lace liri moyo wosatha; cifukwa cace zimene ndilankhula, monga momwe Atate wanena ndi Ine, momwemo ndilankhula.

Werengani mutu wathunthu Yohane 12