Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 12:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pomwepo anatsala masiku asanu ndi limodzi asanafike Paskha, Yesu anadza ku Betaniya kumene kunali Lazaro, amene Yesu adamuukitsa kwa akufa.

2. Ndipo anamkonzera iye cakudya komweko; ndipo Marita anatumikira; koma Lazaro anali mmodzi wa iwo akuseama pacakudya pamodzi ndi iye.

3. Pamenepo Mariya m'mene adatenga muyeso umodzi wa mafuta onunkhira bwino a nardo a mtengo wace wapatali, anadzoza mapazi a Yesu, napukuta mapazi ace ndi tsitsi lace; ndipo nyumba inadzazidwa ndi mnunkho wace wa mafutawo.

4. Koma Yudase Isikariote, mmodzi wa akuphunzira ace, amene adzampereka iye, ananena,

5. Nanga mafuta onunkhira awa sanagulitsidwa cifukwa ninji ndi marupiya atheka mazana atatu, ndi kupatsidwa kwa osauka?

Werengani mutu wathunthu Yohane 12