Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 12:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pomwepo anatsala masiku asanu ndi limodzi asanafike Paskha, Yesu anadza ku Betaniya kumene kunali Lazaro, amene Yesu adamuukitsa kwa akufa.

2. Ndipo anamkonzera iye cakudya komweko; ndipo Marita anatumikira; koma Lazaro anali mmodzi wa iwo akuseama pacakudya pamodzi ndi iye.

3. Pamenepo Mariya m'mene adatenga muyeso umodzi wa mafuta onunkhira bwino a nardo a mtengo wace wapatali, anadzoza mapazi a Yesu, napukuta mapazi ace ndi tsitsi lace; ndipo nyumba inadzazidwa ndi mnunkho wace wa mafutawo.

4. Koma Yudase Isikariote, mmodzi wa akuphunzira ace, amene adzampereka iye, ananena,

5. Nanga mafuta onunkhira awa sanagulitsidwa cifukwa ninji ndi marupiya atheka mazana atatu, ndi kupatsidwa kwa osauka?

6. Koma ananena ici si cifukwa analikusamalira osauka, koma cifukwa anali mbala, ndipo pokhala nalo thumba, amabazoikidwamo.

7. Pamenepo Yesu anati, Mleke iye, pakuti anacisungira ici tsiku la kuikidwa kwanga.

8. Pakuti osauka muli nao pamodzi ndi inu nthawi zonse; koma simuli ndi Ine nthawi zonse.

9. Pamenepo khamu lalikuru la Ayuda Iinadziwa kuti ali pomwepo; ndipo anadza, si cifukwa: ca Yesu yekha, koma kuti adzaone Lazaro, amene adamuukitsa kwa akufa.

10. Koma ansembe akulu anapangana kuti akaphe Lazaronso;

11. pakuti ambiri a Ayuda anacoka cifukwa ca iye, nakhulupirira Yesu.

12. M'mawa mwace khamu lalikuru la anthu amene adadza kuphwando, pakumva kuti Yesu alinkudza ku Yerusalemu,

Werengani mutu wathunthu Yohane 12