Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 10:2-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Koma iye wakulowera pakhomo, ndiye mbusa wa nkhosa.

3. Iyeyu, wapakhomo amtsegulira ndi nkhosa zimva mau ace; ndipo aitana nkhosa za iye yekha maina ao, nazitsogolera kunja.

4. Pamene adaturutsa zonse za iye yekha, azitsogolera; ndi nkhosa zimtsata iye; cifukwa zidziwa mau ace.

5. Koma mlendo sizidzamtsata, koma zidzamthawa; cifukwasizidziwa mau a alendo.

6. Fanizo ili Yesu ananena kwa iwo; koma sanazindikira zimene Yesu analikulankhula nao.

7. Cifukwa cace Yesuananenanso nao, Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Ine ndine khomo la nkhosa.

8. Onse amene anadza m'tsogolo mwa Ine ali akuba, ndi olanda: koma nkhosa sizinamva iwo.

9. Ine ndine khomo; ngati wina alowa ndi Ine, adzapulu-mutsidwa, nadzalowa, nadzaturuka, nadzapeza busa.

10. Siikudza mbala, koma kuti ikabe, ndi kupha, ndi kuononga, Ndadza Ine kuti akhale ndi moyo, ndi kukhala nao wocuruka.

11. Ine ndine Mbusa Wabwino; mbusa wabwino ataya moyo wace cifukwa ca nkhosa.

12. Wolipidwa amene sakhala mbusa, amene nkhosa siziri zace za yekha, aona mmbulu ulinkudza, nasiya nkhosazo, nathawa; ndipo mmbulu uzikwatula, nuzibalalitsa;

13. cifukwa ali wolipidwa, ndipo sasamala nkhosa.

14. Ine ndine Mbusa Wabwino; ndipo ndizindikira zanga, ndi zanga zindizindikira ine,

Werengani mutu wathunthu Yohane 10