Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 1:6-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Kunali munthu, wotumidwa ndi Mulungu, dzina lace ndiye Yohane.

7. Iyeyu anadza mwa umboni kudzacita umboni za kuunikaku, kuti onse akakhulupirire mwa iye,

8. iye sindiye kuunikaku, koma anatumidwa kukacita umboni wa kuunikaku.

9. Uku ndiko kuunika kweni kweni, kumene kuunikira anthu onse akulowa m'dziko lapansi.

10. Anali m'dziko lapansi, ndi dziko linalengedwa ndi iye, koma dziko silinamzindikira iye.

11. Anadza kwa zace za iye yekha, ndipo ace a mwini yekha sanamlandira iye.

12. Koma onse amene anamlandira iye, kwa iwo anapatsa mphamvu yakukhala ana a Mulungu, kwa iwotu, akukhulupirira dzina lace;

13. amene sanabadwa ndi mwazi, kapena ndi cifuniro ca thupi, kapena ndi cifuniro ca munthu, koma ca Mulungu.

14. Ndipo Mau anasandulika thupi, nakhazikika pakati pa ife, ndipo tinaona ulemerero wace, ulemerero wonga wa wobadwa yekha wa Atate, wodzala ndi cisomo ndi coonadi.

15. Yohane acita umboni za iye, napfuula nati, Uyu ndiye amene ndinanena za iye, Wakudzayo pambuyo panga analipo ndisanabadwe ine; cifukwa anakhala woyamba wa ine.

16. Cifukwa mwa kudzala kwace tinalandira ife tonse, cisomo cosinthana ndi cisomo.

17. Cifukwa cilamulo cinapatsidwa mwa Mose; cisomo ndicoonadi zinadza mwa Yesu Kristu.

18. Kulibe munthu anaona Mulungu nthawi zonse; Mwana wobadwa yekha wakukhala pa cifuwa ca Atate, Iyeyu anafotokozera.

19. Ndipo umene ndiwo umboni wa Yohane, pamene Ayudaanatuma kwa iye ansembe ndi alembi a ku Yerusalemu akamfunse iye, Ndiwe yani?

20. Ndipo anabvomera, wosakana; nalola kuti, Sindine Kristu.

21. Ndipo anamfunsa iye, Nanga bwanji? ndiwe Eliya kodi? Nanena iye, Sindine iye, Ndiwe Mneneriyo kodi? Nayankha, Iai.

22. Cifukwa cace anati kwa iye, Ndiwe yani? kuti tibwezere mau kwa iwo anatituma ife. Unena ciani za iwe wekha?

23. Anati, 1 Ndine mau a wopfuula m'cipululu, Lungamitsani njira ya Mbuye, monga anati Yesaya mneneriyo.

24. Ndipo otumidwawo analia kwa Marisi.

25. Ndipo anamfunsa iye, nati kwa iye, Koma ubatiza bwanji, ngati suli Kristu, kapena Eliya, kapena Mneneriyo?

Werengani mutu wathunthu Yohane 1