Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 1:30-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. 6 Ndiye amene ndinati za iye, Pambuyo panga palinkudza munthu amene analipo ndisanabadwe ine; pakuti anali woyamba wa ine.

31. Ndipo sindinamdziwa iye; koma kuti aonetsedwe kwa Israyeli, 7 cifukwa ca ici ndinadzaine kudzabatiza ndi madzi.

32. Ndipo Yohane anacita umboni, nati, 8 Ndinaona Mzimu alikutsika kucokera Kumwamba monga nkhunda; nakhalabe pa iye.

33. Ndipo sindinamdziwa iye, koma wonditumayo kudzabatiza ndi madzi, Iyeyu ananena ndi ine, Amene udzaona Mzimu atsikira, nakhala pa iye, 9 yemweyu ndiye wakubatiza ndi Mzimu Woyera.

34. Ndipo ndaona ine, ndipo ndacita umboni kuti Mwana wa Mulungu ndi Yemweyu.

35. M'mawa mwacenso analikuimirira Yohane ndi awiri a akuphunzira ace;

36. ndipo poyang'ana Yesu alikuyenda, anati, 10 Onani Mwanawankhosa wa Mulungu!

37. Ndipo akuphunzira awiriwo anamva iye alinkulankhula, natsata Yesu.

38. Koma Yesu anaceuka, napenya iwo alikumtsata, nanena nao, Mufuna ciani? Ndipo anati kwa iye, Rabi (ndiko kunena posandulika, Mphunzitsi), mukhala kuti?

39. Nanena nao, Tiyeni, mukaone, Pamenepo anadza naona kumene anakhala; nakhala ndi iye tsiku lomwelo; panali monga ora lakhumi.

Werengani mutu wathunthu Yohane 1