Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 1:22-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Cifukwa cace anati kwa iye, Ndiwe yani? kuti tibwezere mau kwa iwo anatituma ife. Unena ciani za iwe wekha?

23. Anati, 1 Ndine mau a wopfuula m'cipululu, Lungamitsani njira ya Mbuye, monga anati Yesaya mneneriyo.

24. Ndipo otumidwawo analia kwa Marisi.

25. Ndipo anamfunsa iye, nati kwa iye, Koma ubatiza bwanji, ngati suli Kristu, kapena Eliya, kapena Mneneriyo?

26. Yohane anawayankha, nati, 2 Ine ndibatiza ndi madzi; pakati pa inu paimirira amene simumdziwa,

27. 3 ndiye wakudza pambuyo panga, amene sindiyenera kummasulira lamba la nsapato yace.

28. Zinthu izi zinacitika m'Betaniya tsidya lija la Y ordano, pomwe analikubatiza Yohane.

29. M'mawa mwace anaona Yesu alinkudza kwa iye, nanena, 4 Onani Mwanawankhosa wa Mulungu 5 amene acotsa cimo lace la dziko lapasi!

30. 6 Ndiye amene ndinati za iye, Pambuyo panga palinkudza munthu amene analipo ndisanabadwe ine; pakuti anali woyamba wa ine.

31. Ndipo sindinamdziwa iye; koma kuti aonetsedwe kwa Israyeli, 7 cifukwa ca ici ndinadzaine kudzabatiza ndi madzi.

32. Ndipo Yohane anacita umboni, nati, 8 Ndinaona Mzimu alikutsika kucokera Kumwamba monga nkhunda; nakhalabe pa iye.

33. Ndipo sindinamdziwa iye, koma wonditumayo kudzabatiza ndi madzi, Iyeyu ananena ndi ine, Amene udzaona Mzimu atsikira, nakhala pa iye, 9 yemweyu ndiye wakubatiza ndi Mzimu Woyera.

34. Ndipo ndaona ine, ndipo ndacita umboni kuti Mwana wa Mulungu ndi Yemweyu.

35. M'mawa mwacenso analikuimirira Yohane ndi awiri a akuphunzira ace;

36. ndipo poyang'ana Yesu alikuyenda, anati, 10 Onani Mwanawankhosa wa Mulungu!

37. Ndipo akuphunzira awiriwo anamva iye alinkulankhula, natsata Yesu.

38. Koma Yesu anaceuka, napenya iwo alikumtsata, nanena nao, Mufuna ciani? Ndipo anati kwa iye, Rabi (ndiko kunena posandulika, Mphunzitsi), mukhala kuti?

Werengani mutu wathunthu Yohane 1