Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 1:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Cifukwa cilamulo cinapatsidwa mwa Mose; cisomo ndicoonadi zinadza mwa Yesu Kristu.

18. Kulibe munthu anaona Mulungu nthawi zonse; Mwana wobadwa yekha wakukhala pa cifuwa ca Atate, Iyeyu anafotokozera.

19. Ndipo umene ndiwo umboni wa Yohane, pamene Ayudaanatuma kwa iye ansembe ndi alembi a ku Yerusalemu akamfunse iye, Ndiwe yani?

20. Ndipo anabvomera, wosakana; nalola kuti, Sindine Kristu.

Werengani mutu wathunthu Yohane 1