Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 1:13-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. amene sanabadwa ndi mwazi, kapena ndi cifuniro ca thupi, kapena ndi cifuniro ca munthu, koma ca Mulungu.

14. Ndipo Mau anasandulika thupi, nakhazikika pakati pa ife, ndipo tinaona ulemerero wace, ulemerero wonga wa wobadwa yekha wa Atate, wodzala ndi cisomo ndi coonadi.

15. Yohane acita umboni za iye, napfuula nati, Uyu ndiye amene ndinanena za iye, Wakudzayo pambuyo panga analipo ndisanabadwe ine; cifukwa anakhala woyamba wa ine.

16. Cifukwa mwa kudzala kwace tinalandira ife tonse, cisomo cosinthana ndi cisomo.

17. Cifukwa cilamulo cinapatsidwa mwa Mose; cisomo ndicoonadi zinadza mwa Yesu Kristu.

18. Kulibe munthu anaona Mulungu nthawi zonse; Mwana wobadwa yekha wakukhala pa cifuwa ca Atate, Iyeyu anafotokozera.

19. Ndipo umene ndiwo umboni wa Yohane, pamene Ayudaanatuma kwa iye ansembe ndi alembi a ku Yerusalemu akamfunse iye, Ndiwe yani?

20. Ndipo anabvomera, wosakana; nalola kuti, Sindine Kristu.

21. Ndipo anamfunsa iye, Nanga bwanji? ndiwe Eliya kodi? Nanena iye, Sindine iye, Ndiwe Mneneriyo kodi? Nayankha, Iai.

22. Cifukwa cace anati kwa iye, Ndiwe yani? kuti tibwezere mau kwa iwo anatituma ife. Unena ciani za iwe wekha?

23. Anati, 1 Ndine mau a wopfuula m'cipululu, Lungamitsani njira ya Mbuye, monga anati Yesaya mneneriyo.

Werengani mutu wathunthu Yohane 1