Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yakobo 5:9-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Musaipidwe wina ndi mnzace, abale, kuti mungaweruzidwe. Taonani, woweruza aima pakhomo.

10. Tengani, abale, citsanzo ca kumva zowawa ndi kuleza mtima, aneneri ameneanalankhulam'dzina la Ambuyeo

11. Taonani tiwayesera odala opirirawo; mudamva za cipiriro ca Yobu, ndipo mwaona citsiriziro ca Ambuye, kuti Ambuye ali wodzala cikondi, ndi wacifundo.

12. Koma makamaka, abale anga, musalumbire, kungakhale kuchula mwamba kapena dziko, kapena lumbiro lina liri lonse; koma inde wanu akhale inde, ndi iai wanu akha; le iai; kuti mungagwe m'ciweruziro.

13. Kodi wina wa inu akumva zowawa? Apemphere, Kodi wina asekera? Ayimbire.

14. Pali wina kodi adwala mwa inu? Adziitanire akuru a Mpingo, ndipo apemphere pa iye, atamdzoza ndi mafuta m'dzina la Ambuye:

15. ndipo pemphero la cikhulupiriro lidzapulumutsa wodwalayo, ndipo Ambuye adzamuukitsa; ndipo ngati adacita macimo adzakhululukidwa kwa iye.

Werengani mutu wathunthu Yakobo 5