Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yakobo 2:8-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Koma ngati mucita cikwanirire lamulolo lacifumu, monga mwa malembo, Uzikonda mnzako monga udzikonda wekha, mucita bwino:

9. koma ngati musamala maonekedwe, mucita ucimo, ndipo mutsutsidwa ndi cilamulo monga olakwa.

10. Pakuti amene ali yense angasunge malamulo onse, koma akakhumudwa pa limodzi, iyeyu wacimwira onse.

11. Pakuti Iye wakuti, Usacite cigololo, anatinso, Usaphe. Ndipo ukapanda kucita cigololo, koma ukapha, wakhala wolakwira lamulo.

12. Lankhulani motero, ndipo citani motero, monga anthu amene adzaweruzidwa ndi lamulo la ufulu.

13. Pakuti ciweruziro ciribe cifundo kwa iye amene sanacita cifundo; cifundo cidzitamandira kutsutsana naco ciweruziro.

14. Cipindulocace nciani, abale anga, munthu akanena, Ndiri naco cikhulupiriro, koma alibe nchito? Kodi cikhulupiriroco cikhoza kumpulumutsa?

15. Mbale kapena mlongo akakbalawausiwa, nieikamsowa cakudya ca tsiku lace,

16. ndipo wina wa inu akanena nao, Mukani ndi mtendere, muitapfunde ndi kukhuta; osawapatsa iwo zosowa za pathupi; kupindula kwace nciani?

17. Momwemonso cikhulupiriro, cikapanda kukhala nazo nchito, cikhala cakufa m'kati mwacemo.

18. Koma wina akati, Iwe uli naco cikhulupiriro, ndipo ine ndiri nazo nchito; undionetse ine cikhulupiriro cako copanda nchito zako, ndipo ine ndidzakuonetsa iweeikhulupiriro canga coturuka m'nchito zanga.

19. Ukhulupirira iwe kuti Mulungu ali mmodzi; ucita bwino; ziwanda zikhulupiranso, ndipo zinthunthumira.

20. Koma ufuna kuzindikira kodi, munthu wopanda pace iwe, kuti cikhulupiriro copanda nchito ciri cabe?

21. Abrabamu kholo lathu, sanayesedwa wolungama ndi nchito kodi, paja adapereka mwana wace Isake nsembe pa guwa la nsembe?

22. Upenya kuti cikhulupiriro cidacita pamodzi ndi nchito zace, ndipo moturuka mwa nchito cikhulupiriro cidayesedwa cangwiro;

Werengani mutu wathunthu Yakobo 2