Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yakobo 1:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Mwa ici, mutabvula cinyanso conse ndi cisefukiro ca coipa, landirani ndi cifatso mau ookedwa mwa inu, okhoza kupulumutsa moyo wanu.

22. Khalani akucita mau, osati akumva okha, ndi kudzinyenga nokha.

23. Pakuti ngati munthu ali wakumva mau wosati wakucita, iyeyu afanana ndi munthu wakuyang'anira nkhope yace ya cibadwidwe cace m'kalirole;

24. pakuti wadziyang'anira yekha nacoka, naiwala pompaja nali wotani.

Werengani mutu wathunthu Yakobo 1