Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Tito 1:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Umboni uwu uli woona. Mwa ici uwadzudzule mokaripa, kuti akakhale olama m'cikhulupiriro,

14. osasamala nthanu zacabe za Ciyuda, ndi malamulo a anthu opatuka kusiyana naco coonadi.

15. Zonse ziyera kwa iwo amene ayera mtima; koma kwa iwo odetsedwa ndi osakhulupira kulibe kanthu koyera; komatu zadetsedwa nzeru zao ndi cikumbu mtima cao.

16. Abvomereza kuti adziwa Mulungu, koma ndi Debito zao amkana iye, popeza ali onyansitsa, ndi osamvera, ndi pa nchito zonse zabwino osatsimikizidwa.

Werengani mutu wathunthu Tito 1