Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 9:6-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Pakuti sanadziwa cimene adzayankha; cifukwa anacita mantha ndithu.

7. Ndipo panadza mtambo wakuwaphimba iwo; ndipo mau munaturuka m'mtambomo, kuti, Uyu ndiye Mwana wanga wokondedwa; mverani Iye.

8. Ndipo dzidzidzi pounguzaunguza, sanapenya munthu wina yense, koma Yesu yekha, ndi iwo eni.

9. Ndipo pakutsika iwo paphiri, Iye anawalamulira kuti asauze munthu zinthu zimene adaziona, koma pamene Mwana wa munthu akadzauka kwa akufa ndipo.

10. Ndipo anasunga mauwo, nafunsana mwa iwo okha, kuti, Kuuka kwa akufa nciani?

11. Ndipo anamfunsa Iye, nanena, Nanga alembi anena kuti adzayamba kufika Eliya?

12. Ndipo Iye ananena nao, Eliya ayamba kudza ndithu, nadzakonza zinthu zonse; ndipo kwalembedwa bwanji za Mwana wa munthu, kuti ayenera kumva zowawa zambiri ndi kuyesedwa cabe?

13. Koma ndinena ndi inu kuti anafikadi Eliya, ndipo anamcitiranso ziri zonse iwo anazifuna, monga kwalembedwa za iye.

14. Ndipo pamene anadza kwa ophunzira, anaona khamu lalikuru la anthu ozungulira iwo, ndi alembi alikufunsana nao.

15. Ndipo pomwepo anthu onse a khamulo, pakumuona Iye, anazizwa kwambiri, namthamangira Iye, namlankhula.

16. Ndipo anawafunsa iwo, Mufunsa na nao ciani?

17. Ndipo wina wa m'khamulo anamyankha Iye, kuti, Mphunzitsi, ndadza naye kwa Inu mwana wanga, ali nao mzimu wosalankhula;

18. ndipo ponse pamene umgwira, umgwetsa; ndipo acita thobvu, nakukuta mano, nanyololoka; ndipo ndinalankhula nao ophunzira anu kuti auturutse; koma sanakhoza.

19. Ndipo Iye anawayankha nanena, Mbadwo wosakhulupirira inu, ndidzakhala ndi inu kufikira liti? ndidzakulekererani nthawi yanji? Mudze naye kwa Ine.

20. Ndipo anadza naye kwa Iye; ndipo pakumuona, pomwepo mzimuwo unamng'amba koopsya; ndipo anagwa pansi nabvimbvinika ndi kucita thobvu.

21. Ndipo Iye anafunsa atate wace, kuti, Cimeneci cinayamba kumgwira liti? Ndipo anati, Cidamyamba akali mwana.

22. Ndipo kawiri kawiri ukamtaya kumoto ndi kumadzi, kumuononga; koma ngati mukhoza kucita kanthu mtithandize, ndi kuticitira cifundo.

23. Ndipo Yesu ananena naye, Ngati mukhoza! Zinthu zonse zitheka ndi iye wakukhulupirira.

24. Pomwepo atate wa mwana anapfuula, nanena, Ndikhulupirira; thandizani kusakhulupirira kwanga.

Werengani mutu wathunthu Marko 9