Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 9:31-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Pakuti anaphunzitsa ophunzira ace, nanena nao, kuti, Mwana wa munthu aperekedwa m'manja a anthu, ndipo adzamupha Iye; ndipo ataphedwa, adzauka pofika masiku atatu.

32. Koma iwo sanazindikira mauwo, naopa kumfunsa.

33. Ndipo iwo anadza ku Kapernao; ndipo pamene anakhala m'nyumba, Iye anawafunsa, Munalikutsutsana ninji panjira?

34. Koma iwo anakhala cete; pakuti anatsutsana wina ndi mnzace panjira, kuti, wamkuru ndani?

Werengani mutu wathunthu Marko 9