Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 9:26-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Ndipo pamene unapfuula, numng'ambitsa, unaturuka; ndipo mwana anakhala ngati wakufa; kotero kuti ambiri ananena, Wamwalira.

27. Koma Yesu anamgwira dzanja lace, namnyamutsa; ndipo anaimirira.

28. Ndipo pamene Iye adalowa m'nyumba, ophunzira ace anamfunsa m'tseri, kuti, Nanga bwanji sitinakhoza ife kuuturutsa?

29. Ndipo Iye anati kwa iwo, Mtundu uwu sukhoza kuturuka ndi kanthu kena konse, koma ndi kupemphera.

Werengani mutu wathunthu Marko 9