Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 9:24-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Pomwepo atate wa mwana anapfuula, nanena, Ndikhulupirira; thandizani kusakhulupirira kwanga.

25. Ndipo pamene Yesu anaona kuti khamu la anthu lirikuthamangira pamodzi, anadzudzula mzimu woipawo, nanena ndi uwo, Mzimu wosalankhula ndi wogontha iwe, Ine ndikulamula iwe, turuka mwa iye, ndipo usalowenso mwa iye.

26. Ndipo pamene unapfuula, numng'ambitsa, unaturuka; ndipo mwana anakhala ngati wakufa; kotero kuti ambiri ananena, Wamwalira.

27. Koma Yesu anamgwira dzanja lace, namnyamutsa; ndipo anaimirira.

28. Ndipo pamene Iye adalowa m'nyumba, ophunzira ace anamfunsa m'tseri, kuti, Nanga bwanji sitinakhoza ife kuuturutsa?

Werengani mutu wathunthu Marko 9