Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 9:15-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo pomwepo anthu onse a khamulo, pakumuona Iye, anazizwa kwambiri, namthamangira Iye, namlankhula.

16. Ndipo anawafunsa iwo, Mufunsa na nao ciani?

17. Ndipo wina wa m'khamulo anamyankha Iye, kuti, Mphunzitsi, ndadza naye kwa Inu mwana wanga, ali nao mzimu wosalankhula;

18. ndipo ponse pamene umgwira, umgwetsa; ndipo acita thobvu, nakukuta mano, nanyololoka; ndipo ndinalankhula nao ophunzira anu kuti auturutse; koma sanakhoza.

19. Ndipo Iye anawayankha nanena, Mbadwo wosakhulupirira inu, ndidzakhala ndi inu kufikira liti? ndidzakulekererani nthawi yanji? Mudze naye kwa Ine.

20. Ndipo anadza naye kwa Iye; ndipo pakumuona, pomwepo mzimuwo unamng'amba koopsya; ndipo anagwa pansi nabvimbvinika ndi kucita thobvu.

21. Ndipo Iye anafunsa atate wace, kuti, Cimeneci cinayamba kumgwira liti? Ndipo anati, Cidamyamba akali mwana.

22. Ndipo kawiri kawiri ukamtaya kumoto ndi kumadzi, kumuononga; koma ngati mukhoza kucita kanthu mtithandize, ndi kuticitira cifundo.

23. Ndipo Yesu ananena naye, Ngati mukhoza! Zinthu zonse zitheka ndi iye wakukhulupirira.

24. Pomwepo atate wa mwana anapfuula, nanena, Ndikhulupirira; thandizani kusakhulupirira kwanga.

Werengani mutu wathunthu Marko 9