Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 9:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo ananena nao, Ndithu ndinena ndi inu kuti, Alipo ena akuimirira pano, amene sadzalawa imfa konse, kufikira akaona Ufumu wa Mulungu utadza ndi mphamvu.

2. Ndipo atapita masiku asanu ndi limodzi, Yesu anatenga Petro, ndi Yakobo, ndi Yohane, nakwera nao pa phiri lalitali padera pa okha; ndipo anasandulika pamaso pao:

3. ndipo zobvala zace zinakhala zonyezimira, zoyera mbu; monga ngati muomba wotsuka nsaru pa dziko lapansi sangathe kuziyeretsai.

Werengani mutu wathunthu Marko 9