Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 6:16-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Koma Herode pamene anamva, ananena, Yohane amene ndamdula mutu, wauka iyeyo.

17. Pakuti Herode, mwini yekha, adatuma anthu namgwira Yohane, nammanga m'nyumba yandende, cifukwa ca Herodiya, mkazi wa Filipo mbale wace; cifukwa adamkwatira iye.

18. Pakuti Yohane adanena kwa Herode, Si kuloledwa kwa inu kukhala naye mkazi wa mbale wanu.

19. Ndipo Herodiya anamuda, nafuna kumupha; koma sanakhoza;

20. pakuti Herode anaopa Yohane, podziwa kuti ali munthu wolungama ndi woyera mtima, ndipo anamsunga iye. Ndipo pamene anamva iye anathedwa nzeru, oakondwa kumva iye.

Werengani mutu wathunthu Marko 6