Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 6:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo pamalo ponse sakulandirani, kapena kumvera inu, pakucoka kumeneko, sansani pfumbi liri ku mapazi anu, likhale mboni ya kwa iwo.

12. Ndipo anaturuka nalalikira kuti anthu atembenuke mitima.

13. Ndipo anaturutsa mizimu yoipa yambiri, nadzoza mafuta anthu ambiri akudwala, nawaciritsa.

14. Ndipo mfumu Herode anamva izi; pakuti dzina lace lidamveka; ndipo ananena, kuti, Yohane Mbatizi wauka kwa akufa, ndipo cifukwa cace mphamvu izi zicitacita mwa Iye.

15. Koma ena ananena, kuti, Ndiye Eliya, Anati enanso, Ndiye mneneri, monga ngati mmodzi wa aneneriwo,

16. Koma Herode pamene anamva, ananena, Yohane amene ndamdula mutu, wauka iyeyo.

Werengani mutu wathunthu Marko 6