Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 14:44-50 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

44. Ndipo wakumpereka Iye anawapatsa cizindikilo, nanena, Iye amene ndidzampsompsona, ndiyetu; mgwireni munke naye cisungire.

45. Ndipo atafika, pomwepo anadza kwa Iye, nanena, Rabi; nampsompsonetsa.

46. Ndipo anamthira manja, namgwira.

47. Koma mmodzi wina wa iwo akuimirirapo, anasolola lupanga lace, nakantha kapolo wace wa mkulu wa ansembe, namdula khutu lace.

48. Ndipo Yesu anayankha nati kwa iwo, Kodi mwaturuka ndi malupanga ndi mikunkhu kundigwira ine monga wacifwamba?

49. Masiku onse ndinali nanu m'Kacisi ndirikuphunzitsa, ndipo simunandigwira Ine; koma ici cacitika kuti malembo akwanitsidwe.

50. Ndipo iwo onse anamsiya Iye, nathawa.

Werengani mutu wathunthu Marko 14