Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 13:4-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Tiuzeni, zinthu izi zidzacitika liti? Ndi cotani cizindikilo cace cakuti ziri pafupi pa kumarizidwa zinthu izi zonse?

5. Ndipo Yesu anayamba kunena nao, Yang'anirani kuti munthu asakusoceretseni.

6. Ambiri adzafika m'dzina langa, nadzanena, Ine ndine Iye; nadzasoceretsa ambiri.

7. Ndipo m'mene mudzamva za nkhondo ndi mbiri zace za nkhondo, musamadera nkhawa: ziyenerakucitika izi; koma sicinafike cimariziro.

8. Pakuti mtundu wa anthu udzayambana ndi mtundu wina, ndipo ufumu ndi ufumu unzace: padzakhaia zibvomezi m'malo m'malo; padzakhala njala; izi ndi zoyambira za zowawa.

9. Koma inu mudziyang'anire inu nokha; pakuti adzakuperekani inu kwa akuru a mirandu; ndipo adzakukwapulani m'masunagoge; ndipo pamaso pa akazembe ndi mafwnu mudzaimirira cifukwa ca Ine, kukhale umboni kwa iwo.

10. Ndipo Uthenga Wabwino uyenera uyambe kulalikidwa kwa anthu a mitundu yonse.

11. Ndipo pamene adzapita nanu kumlandu, nadzakuperekani, musada nkhawa usanayambe mrandu ndi cimene mudzalankhula; koma ci mene cidzapatsidwa kwa inu m'mphindi yomweyo, mucilankhule; pakuti olankhula si ndinu, koma Mzimu Woyera.

12. Ndipo mbale adzapereka mbale wace kuti amuphe, ndi atate mwana wace; ndi ana adza yambana ndi akuwabala, nadzawaphetsa,

13. Ndipo adzada inu anthu onse cifukwa ca dzina langa: koma iye wakupirira kufikira cimariziro, yemweyo adzapulumutsidwa.

14. Ndipo pamene mukaona conyansa ca kupululutsa cirikuima pomwe siciyenera (wakuwerenga azindikile), pamenepo a m'Yudeya athawire kumapiri;

15. ndi iye amene ali pamwamba pa chindwi asatsike, kapena asalowe kukaturutsa kanthu m'nyumba mwace;

16. ndi iye amene ali kumunda asabwere kudzatenga Malaya ace.

17. Koma tsoka iwo akukhala ndi pakati, ndi akuyamwitsa ana masiku awol

18. Ndipo pempherani kuti kusakhale m'nyengo yacisanu.

19. Pakuti masiku aja padzakhala cisautso, conga sicinakhala cinzace kuyambira ciyambi ca cilengedwe cimene Mulungu anacilenga ndi kufikira tsopano, ndipo sicidzakhalanso nthawi zonse.

20. Ndipo Ambuye akadapanda kufupikitsa masikuwo, sakadapulumuka munthu mmodzi yense; koma cifukwa ca osankhidwa amene anawasankha, anafupikitsa masikuwo.

21. Ndipo pamenepo wina akati kwa inu, Onani Kristu ali pano; kapena, Onani, uko; musabvomereze;

Werengani mutu wathunthu Marko 13