Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 13:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo pamene analikuturuka Iye m'Kacisi, mmodzi wa ophunzira ace ananena kwa Iye, Mphunzitsi, onani, miyala yotere ndi nyumba yotere.

2. Ndipo Yesu anati kwa iye, Kodi waona nyumba izi zazikuru? Sudzasiyidwa pano mwala umodzi pamwamba pa unzace, umene sudzagwetsedwa.

3. Ndipo pamene anakhala Iye pa phiri la Azitona, popenyana ndi Kacisi, anamfunsa Iye m'tseri Petro, ndi Yakobo, ndi Yohane, ndi Andreya, kuti,

4. Tiuzeni, zinthu izi zidzacitika liti? Ndi cotani cizindikilo cace cakuti ziri pafupi pa kumarizidwa zinthu izi zonse?

5. Ndipo Yesu anayamba kunena nao, Yang'anirani kuti munthu asakusoceretseni.

6. Ambiri adzafika m'dzina langa, nadzanena, Ine ndine Iye; nadzasoceretsa ambiri.

7. Ndipo m'mene mudzamva za nkhondo ndi mbiri zace za nkhondo, musamadera nkhawa: ziyenerakucitika izi; koma sicinafike cimariziro.

8. Pakuti mtundu wa anthu udzayambana ndi mtundu wina, ndipo ufumu ndi ufumu unzace: padzakhaia zibvomezi m'malo m'malo; padzakhala njala; izi ndi zoyambira za zowawa.

9. Koma inu mudziyang'anire inu nokha; pakuti adzakuperekani inu kwa akuru a mirandu; ndipo adzakukwapulani m'masunagoge; ndipo pamaso pa akazembe ndi mafwnu mudzaimirira cifukwa ca Ine, kukhale umboni kwa iwo.

10. Ndipo Uthenga Wabwino uyenera uyambe kulalikidwa kwa anthu a mitundu yonse.

Werengani mutu wathunthu Marko 13