Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 12:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo anatumanso kapolo wina kwa iwo; ndipo ameneyu anamlasa mutu, namcitira zomcititsa manyazi.

5. Ndipo anatuma wina; iyeyu anamupha; ndi ena ambiri; ena anawapanda, ndi ena anawapha.

6. Anamtsalira mmodzi, ndiye mwana wace wokondedwa; potsiriza anamtuma iye kwa iwo, nanena, Adzamcitira ulemu mwana wanga.

7. Koma olima ajawo, ananena mwa iwo okha, Ameneyu ndiye wolowa nyumba; tiyeni timuphe iye, ndipo mundawu udzakhala wathu.

8. Ndipo anamtenga, namupha iye, namtaya kunja kwa munda.

Werengani mutu wathunthu Marko 12