Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 12:10-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Kodi simunawerenga ngakhale lembo ili;Mwala umene anaukana omanga nyumba,Womwewu unayesedwa mutu wa pangondya:

11. Ici cinacokera kwa Ambuye, Ndipo ciri cozizwitsa m'maso mwathu?

12. Ndipo anayesa kumgwira Iye; koma anaopa khamu la anthu, pakuti anazindikira kuti Iye anakamba fanizo ili kuwatsutsa iwo; ndipo anamsiya Iye, nacoka.

13. Ndipo anatuma kwa Iye ena a Afarisi ndi a Aherode, kuti akamkole Iye m'kulankhula kwace.

14. Ndipo pamene anafika, ananena naye, Mphunzitsi, tidziwa kuti muli woona, ndipo simusamala munthu; pakuti simuyang'ana nkhope ya anthu, koma muphunzitsa njira ya Mulungu moona: Nkuloleka kodi kupereka msonkho kwa Kaisara, kapena iai?

15. Kodi tipereke kapena tisapereke? Koma Iye anadziwa cinyengo cao, nati kwa iwo, Mundiyeseranji? Nditengereni rupiya latheka, kuti ndilione. Ndipo analitenga.

16. Ndipo ananena nao, Cithunzithunzi ici, ndi cilembo cace ziri za yani? Ndipo anati kwa Iye, Za Kaisara.

17. Ndipo Yesu anati kwa iwo, Perekani zace za Kaisara kwa Kaisara, ndi zace za Mulungu kwa Mulungu. Ndipo anazizwa naye kwambiri.

Werengani mutu wathunthu Marko 12