Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 9:12-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. ndipo anaona mwamuna dzina, lace Hananiya, alikulowa, namuika manja, kuti apenyenso.

13. Ndipo Hananiya anayankha nati, Ambuye ndamva ndi ambiri za munthu uyu kuti anacitiradi coipa oyera mtima anu m'Yerusalemu;

14. ndi kuti pane ali nao ulamuliro wa kwa ansembe akulu wakumanga onse akuitana pa dzina lanu.

15. Koma Ambuye anat kwa iye, Pita; pakuti iye ndiye cotengera canga cosankhika, cakunyamula dzina langa pamaso pa amitundu ndi mafumu ndi ana a Israyeli;

16. pakuti Ine ndidzamuonetsa iye zinthu zambirl ayenera iye kuzimva kuwawa cifukwaca dzina langa.

17. Ndipo anacoka Hananiya, nalowa m'nyumbayo; ndipo anaika manja ace pa iye, nati, Saulo, mbale, Ambuye wandituma ine, ndiye Yesu amene anakuonekerani pa njira wadzerayo, kuti upenyenso, ndi kudzazidwa ndi Mzimu Woyera.

18. Ndipo pomwepo padagwa kucoka m'maso mwace ngati mamba, ndipo anapenyanso;

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 9